Genesis 11:12-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo Aripakasadi anakhala ndi moyo zaka makumi atatu kudza zisanu, nabala Sela;

13. ndipo Aripakasadi anakhala ndi moyo zaka mazana anai kudza zitatu, atabala Sela, nabala ana amuna ndi akazi.

14. Ndipo Sela anakhala ndi moyo zaka makumi atatu, nabala Ebere;

15. ndipo Sela anakhala ndi moyo zaka mazana anai kudza zitatu, atabala Ebere, nabala ana amuna ndi akazi.

16. Ndipo Ebere anakhala ndi moyo zaka makumi atatu kudza zinai, nabala Pelege;

17. ndipo Ebere anakhala ndi moyo zaka mazana anai kudza makumi awiri, atabala Pelege, nabala ana amuna ndi akazi.

18. Ndipo Pelege anakhala ndi moyo zaka makumi atatu, nabala, Reu;

Genesis 11