Ezekieli 7:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Atero Yehova Mulungu, Coipa, coipa ca pa cokha, taona cirinkudza.

6. Kutha kwafika, kwafika kutha, kwakugalamukira, taona kwafika.

7. Tsoka lako lakufikira, nzika iwe, yafika nthawi, tsiku liri pafupi, ndilo laphokoso, si lakupfuula mokondwera kumapiri,

8. Katsala kamphindi, ndipo ndidzakutsanulira ukali wanga, ndi kukukwaniritsira mkwiyo wanga, ndi kukuweruza monga mwa njira zako, ndipo ndidzakubwezera zonyansa zako zonse.

9. Ndipo diso langa silidzalekerera, wosacita cifundo Ine, ndidzakubwezera monga mwa njira zako, ndi zonyansa zako zidzakhala pakati pako; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova wakukantha.

10. Taona, tsikuli, taona, lafika; tsoka lako laturuka, ndodo yaphuka mphundu za maluwa, kudzitama kwaphuka.

Ezekieli 7