14. Yairi mwana wa Manase analanda dziko lonse la Arigobi, kufikira malire a Agesuri ndi Amaakati; nalicha dzina lace, Basana Haroti Yairi, kufikira lero lino.)
15. Ndipo ndinampatsa Makiri Gileadi.
16. Koma ndinapatsa Arubeni ndi Agadi kuyambira ku Gileadi kufikira ku mtsinje wa Arinoni, pakati pa cigwa ndi malire ace, kufikira mtsinje wa Yaboki, ndiwo malire a ana a Amoni;
17. ndi cidikha, ndi Yordano ndi malire ace, kuyambira ku Kinerete kufikira ku nyanja ya kucidikha, ndiyo Nyanja ya Mcere, patsinde pa Pisiga, kum'mawa.
18. Ndipo ndinauza inu muja, ndi kuti, Yehova Mulungu wanu wakupatsani dziko ili likhale lanu lanu, muoloke, amuna onse amphamvu obvala zida zao, pamaso pa abale anu ana a Israyeli.
19. Koma akazi anu, ndi ana anu, ndi zoweta zanu, (ndidziwa muli nazo zoweta zambiri), zikhale m'midzi yanu imene ndinakupatsani;