Deuteronomo 28:32-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. Adzapereka ana anu amuna ndi akazi kwa anthu a mtundu wina, ndipo m'maso mwanu mudzada ndi kupenyerera, powalirira tsiku lonse; koma mulibe mphamvu m'dzanja lanu.

33. Mtundu wa anthu umene simudziwa udzadya zipatso za nthaka yanu ndi nchito zanu zonse; ndipo mudzakhala wopsinjika ndi wophwanyika masiku onse;

34. nimudzakhala oyeruka cifukwa comwe muciona ndi maso anu,

Deuteronomo 28