Danieli 8:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Caka cacitatu ca Belisazara mfumu masomphenya anandionekera kwa ine Danieli, atatha kundionekera oyamba aja.

2. Ndipo ndinaona m'masomphenya; tsono kunali, pakuwaona ine ndinali m'Susani, m'nyumba ya mfumu, ndiwo m'dziko la Elamu; ndinaona m'masomphenya kuti ndinali kumtsinje Ulai.

3. Ndipo ndinakweza maso anga ndi kupenya; taonani, panaima pamtsinje nkhosa yamphongo yokhala nazo nyanga ziwiri, ndi nyanga ziwirizo zinali za msinkhu wautali, koma imodzi inaposa inzace; yoposayo inaphuka m'mbuyo.

Danieli 8