Danieli 11:21-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndi m'malo mwace adzauka munthu woluluka, amene anthu sanampatsa ulemu wa ufumu, koma adzafika kacetecete, nadzalanda ufumu ndi mau osyasyalika.

22. Ndipo mwa mayendedwe ace a cigumula adzakokololedwa pamaso pace, nadzatyoledwa, ngakhale kalonga yemwe wa cipangano.

23. Ndipo atapangana naye adzacita monyenga; pakuti adzakwera, nadzasanduka wamphamvu ndi anthu owerengeka.

24. Adzafika kacetecete ku minda yokometsetsa ya derali, nadzacita cosacita atate ace, kapena makolo ace; adzawawazira zofunkha, ndi zankhondo, ndi cuma, nadzalingiririra malinga ziwembu zace; adzatero nthawi.

25. Nadzautsa mphamvu yace ndi mtima wace ayambane ndi mfumu ya kumwela ndi khamu lalikuru la nkhondo; ndi mfumu ya kumwela ndi khamu lalikuru ndi lamphamvu ndithu; koma sadzaimika, popeza adzamlingiririra ziwembu.

26. Inde iwo akudyako cakudya cace adzamuononga; ndi ankhondo ace adzasefukira, nadzagwaambiri ophedwa.

Danieli 11