Amosi 4:4-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Idzani ku Beteli, mudzalakwe ku Giligala, nimucurukitse zolakwa, nimubwere nazo nsembe zanu zophera m'mawa ndi m'mawa, magawo anu akhumi atapita masiku atatu atatu;

5. nimutenthe nsembe zolemekeza zacotupitsa, nimulalikire nsembe zaufulu, ndi kuzimveketsa; pakuti ici mucikonda, inu ana a Israyeli, ati Ambuye Yehova.

6. Ndipo ine ndakupatsaninso mano oyera m'midzi yanu yonse, ndi kusowa mkate m'malo mwanu monse; koma simunabwerera kudza kwa Ine, ati Yehova.

7. Ndipo Ine ndakumanani mvula, itatsala miyezi itatu isanafika nyengo yakukolola; ndipo ndinabvumbistira mudzi umodzi mvula, osabvumbitsira mudzi wina; munda wina unabvumbidwa mvula, ndi m'munda mosabvumbidwa mvula munafota.

8. M'mwemo midzi iwiri kapena itatu inayenda peyupeyu ku mudzi umodzi kukamwa madzi, koma sanakhuta; koma simunai bwerera kudza kwa Ine, ati Yehova.

9. Ndinakukanthani ndi cinsikwi ndi cinoni; minda yanu yocuruka yamipesa, ndi yamikuyu, ndi yaazitona, yaonongeka ndi cirimamine; koma simunabwerera kudza kwa Ine, ati Yehova.

10. Ndinatumiza mliri pakati panu monga m'Aigupto; anyamata anu ndawapha ndi lupanga, ndi kutenga akavalo anu; ndipo ndinakweretsa kununkha kwa cigono canu kufikitsa kumphuno kwanu; ikoma simunabwerera kudzakwa Ine, ati Yehova.

11. Ndinagubuduza ena mwa inu, monga umo Mulungu anagubuduzira Sodomu ndi Gomora; ndipo inu munali ngati muuni wofumulidwa kumoto; koma simunabwerera kudza kwa Ine, ati Yehova.

Amosi 4