Ahebri 4:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Cifukwa cace tiope kuti kapena likatsala lonjezano lakulowa mpumulo wace, wina wa inu angaoneke ngati adaliperewera.

2. Pakuti kwa ifenso walalikidwa Uthenga Wabwino, monganso kwa iwo; koma iwowa sanapindula nao mau omvekawo, popeza sanasanganizika ndi cikhulupiriro mwa iwo amene adawamva.

3. Popeza ife amene takhulupira tilowa mpumulowo, monga momwe ananena,Monga ndalumbira mu mkwiyowanga,Ngati adzalowa mpumulo wanga:zingakhale nebitozo zidatsirizika kuyambira kuzika kwa dziko lapansi.

Ahebri 4