2 Samueli 3:8-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Pomwepo Abineri anapsa mtima kwambiri pa mau a Isiboseti, nati, Ndine mutu wa gam wa Yuda kodi? Lero lino ndirikucitira zokoma nyumba ya Sauli atate wanu, ndi abale ace, ndi abwenzi ace, ndipo sindinakuperekani m'dzanja la Davide, koma mundinenera lero lino za kulakwa naye mkazi uyu.

9. Mulungu alange Abineri, naonjezepo, ndikapanda kumcitira Davide monga Yehova anamlumbirira;

10. kucotsa ufumu ku nyumba ya Sauli ndi kukhazika mpando wadfumu wa Davide pa Israyeli ndi pa Yuda, kuyambira ku Dani kufikira ku Beereseba.

11. Ndipo iye sanakhoza kuyankha Abineri mau amodzi cifukwa ca kumuopa iye.

2 Samueli 3