2 Samueli 2:12-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo Abineri mwana wa Neri ndi anyamata a Isiboseti mwana wa Sauli anaturuka ku Mahanaimu kunka ku Gibeoni.

13. Ndi Yoabu mwana wa Zeruya, ndi anyamata a Davide anaturuka nakomana nao pa thamanda la Gibeoni; nakhala pansi, ena tsidya lino, ndi ena tsidya lija la thamandalo.

14. Ndipo Abineri ananena ndi Yoabu, Aimirire anyamata nasewere pamaso pathu. Nati Yoabu, Aimirire.

15. Pomwepo iwo anaimirira naoloka owerengedwa, khumi ndi awiri a kwa Benjamini, ndi Isiboseti mwana wa Sauli, ndi khumi ndi awiri a anyamata a Davide.

16. Ndipo anagwirana munthu yense kugwira mutu wa mnzace, nagwaza ndi lupanga lace m'nthiti mwa mnzaceo Comweco anagwa limodzi; cifukwa cace malo aja anachedwa Dera la Mipeni la ku Gibeoni.

17. Ndipo tsikulo nkhondo inakula ndithu. Ndi Abineri ndi anthu a Israyeli anathawa pamaso pa anyamata a Davide.

2 Samueli 2