2 Samueli 14:25-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Ndipo m'lsrayeli monse munalibe wina anthu anamtama kwambiri cifukwa ca kukongola kwace monga Abisalomu; kuyambira ku mapazi kufikira pakati pa mutu wace mwa iye munalibe cirema.

26. Ndipo pometa tsitsi lace amameta potsiriza caka, cifukwa tsitsi linamlemerera, cifukwa cace atalimeta anayesa tsitsi la pa mutu wace, napeza masekeli mazana awiri, monga mwa muyeso wa mfumu.

27. Ndipo kwa Abisalomu kunabadwa ana amuna atatu ndi mwana wamkazi mmodzi, dzina lace ndiye Tamara, iye ndiye mkazi wokongola nkhope.

28. Ndipo Abisalomu anakhala ku Yerusalemu zaka ziwiri zathunthu, osaona nkhope ya mfumu.

29. Pamenepo Abisalomu anaitana Yoabu kuti akamtumize iye kwa mfumu; koma anakana kubwera kwa iye; ndipo anamuitananso nthawi yaciwiri, koma anakana kubwera.

2 Samueli 14