25. natumiza ndi dzanja la Natani mneneriyo, namucha dzina lace Wokondedwa ndi Yehova, cifukwa ca Yehova.
26. Ndipo Yoabu anathira nkhondo pa Raba wa ana a Amoni, nalanda mudzi wacifumu.
27. Yoabu natumiza mithenga kwa Davide nati, Ndaponyana ndi Raba, inde ndalanda mudzi wa pamadzi.
28. Cifukwa cace tsono musonkhanitseanthu otsalawo, nimumangire mudziwo zithando, muulande; kuti ine ndingalande mudziwo, ndipo ungachedwe ndi dzina langa.
29. Ndipo Davide anasonkhanitsa anthu onse, napita ku Raba, naponyana nao, naulanda.
30. Nacotsa korona pa mutu wa mfumu yao; kulemera kwace kunali talente wa golidi; ndipo m'menemo munali miyala ya mtengo wapatali; ndipo anamuika pa mutu wa Davide. Iye naturutsa zofunkha za mudziwo zambirimbiri.