2 Mbiri 9:24-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Nabwera nao munthu yense mtulo wace, zipangizo zasiliva, ndi zipangizo zagolidi, zobvala, ndi zobvala za nkhondo, ndi zonunkhira, akavalo, ndi nyuru; momwemo caka ndi caka.

25. Ndipo Solomo anali nazo zipinda zikwi zinai za akavalo ndi magareta, ndi apakavalo zikwi khumi ndi ziwiri; nawaika m'toidzi ya magareta, ndi m'Yerusalemu kwa mfumu.

26. Ndipo analamulira mafumu onse kuyambira ku Firate kufikira ku dziko la Afilisti, ndi ku malire a ku Aigupto.

27. Ndipo mfumu inacurukitsa siliva m'Yerusalemu ngati miyala; ndi mikungudza anailinganiza ndi mikuyu iri kumadambo kucuruka kwace.

2 Mbiri 9