2 Mbiri 31:15-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndi omvera iye ndiwo Edeni, ndi Minyamini, ndi Yesuwa; ndi Semaya, Amariya, ndi Sekaniya, m'midzi ya ansembe, kugawira abale ao m'zigawo zao mokhulupirika, akuru monga ang'ono;

16. pamodzi ndi iwo oyesedwa mwa cibadwidwe ca amuna, kuyambira a zaka zitatu ndi mphambu, kwa ali yense amene adalowa m'nyumba ya Yehova, monga mwa nchito yace pa tsiku lace, kukacita za utumiki wao m'udikiro wao monga mwa zigawo zao;

17. ndi iwo oyesedwa mwa cibadwidwe ca ansembe mwa nyumba za makolo ao, ndi Alevi, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu m'udikiro mwao, monga mwa zigawo zao;

18. ndi iwo oyesedwa mwa cibadwidwe ca ana ao ang'ono onse, akazi ao, ndi ana ao amuna ndi akazi, mwa msonkhano wonse; pakuti m'kukhulupirika kwao anadzipatula akhale opatulika;

19. panalinso amuna mwa ana a Aroni ansembe, okhala m'minda ya kubusa kwa midzi yao, m'mudzi uli wonse, ochulidwa maina ao, agawire amuna onse mwa ansembe, ndi onse mwa Alevi, oyesedwa mwa cibadwidwe magawo ao.

2 Mbiri 31