2 Mbiri 26:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo anthu onse Ayuda anatenga Uziya, ndiye wa zaka khumi mphambu zisanu ndi cimodzi, namlonga ufumu m'malo mwa atate wace Amaziya.

2. Iye anamanga Eloti, naubweza kwa Yuda, mfumu itagona ndi makolo ace.

3. Uziya anali wa zaka khumi mphambu zisanu ndi cimodzi polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka makumi asanu mphambu ziwiri; ndi dzina la mace ndiye Yekoliya wa ku Yerusalemu.

2 Mbiri 26