2 Mbiri 20:34-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. Macitidwe ena tsono adazicita Yehosafati, zoyamba ndi zotsiriza, taonani, zilembedwa m'buku la mau a Yehu mwana wa Hanani, wochulidwa m'buku la mafumu a Israyeli.

35. Zitathaizi, Yehosafati mfumu ya Yuda anaphatikana ndi Ahaziya mfumu ya Israyeli, yemweyo anacita moipitsitsa;

36. naphatikana naye kupanga zombo zomuka ku Tarisi, nazipanga zombozo m'Ezioni Gebere.

37. Pamenepo Eliezeri mwana wa Dodavahu wa Maresa ananenera kumtsutsa Yehosafati, ndi kuti, Popeza waphatikana ndi Ahaziya Yehova wapasula nchito zako. Ndipo zombo zinasweka zosakhoza kumuka ku Tarisi.

2 Mbiri 20