2 Mbiri 18:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Pamenepo mfumu ya Israyeli inaitana mdindo, niti, Katenge msanga Mikaya mwana wa Yimla.

9. Mfumu ya Israyeli tsono ndi Yehosafati mfumu ya Yuda anakhala yense pa mpando wacifumu wace, obvala zobvala zacifumu zao, nakhala pamalo poyera polowera pa cipata ca Samariya; ndi aneneri onse ananenera pamaso pao.

10. Ndipo Zedekiya mwana wa Kenana anadzisulira nyanga zacitsulo, nati, Atero Yehova, Ndi izi udzagunda Aaramu mpaka adatha psiti.

11. Ndi aneneri onse ananenera momwemo, ndi kuti, Kwerani ku Ramoti Gileadi, mudzapindulako; pakuti Yehova adzaupereka m'dzanja la mfumu.

12. Ndipo mthenga wakukaitana Mikaya ananena naye, ndi kuti, Taonani, mau a aneneri anenera mfumu cokoma ngati m'kamwa m'modzi; mau anu tsono akhaletu ngati amodzi a iwowa, nimunene cokoma.

2 Mbiri 18