1. Caka cakhumi mphambu zisanu ndi ziwiri ca Peka mwana wa Remaliya Ahazi mwana wa Yotamu mfumu ya Yuda analowa ufumu wace.
2. Ahazi anali wa zaka makumi awiri polowa ufumu wace, nakhala mfumu zaka khumi mphambu zisanu ndi cimodzi m'Yerusalemu; koma sanacita zoongoka pamaso pa Yehova Mulungu wace, ngati Davide kholo lace;