2 Mafumu 15:11-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Macitidwe ena tsono a Zekariya, taonani, zalembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Israyeli.

12. Awa ndi mau a Yehova anawanena ndi Yehu, ndi kuti, Ana ako kufikira mbadwo wacinai adzakhala pa mpando wacifumu wa Israyeli. Ndipo kunatero momwemo.

13. Salumu mwana wa Yabesi analowa ufumu wace caka ca makumi atatu mphambu zisanu ndi zinai ca Uziya mfumu ya Yuda, nakhala mfumu mwezi umodzi m'Samariya.

2 Mafumu 15