5. Pakuti tilalikira si za ife tokha, koma Kristu Yesu Ambuye, ndi ife tokha akapolo anu, cifukwa ca Kristu.
6. Pakuti Mulungu amene anati, Kuunika kudzawala kuturuka mumdima, ndiye amene anawala m'mitima yathu kutipatsa ciwalitsiro ca cidziwitso ca ulemerero wa Mulungu pankhope pa Yesu Kristu.
7. Koma tiri naco cuma ici m'zotengera zadothi, kuti ukulu woposa wamphamvu ukhale wa Mulungu, wosacokera kwa ife;
8. ndife osautsika monsemo, koma osapsinjika; osinkhasinkha, koma osakhala kakasi;
9. olondoleka, koma osatayika; ogwetsedwa, koma osaonongeka;
10. nthawi zonse tirikusenzasenza m'thupi kufa kwace kwa Yesu, kuti moyonso wa Yesu uoneke m'thupi mwathu.
11. Pakuti ife amene tiri ndi moyo tiperekeka kuimfa nthawi zonse, cifukwa ca Yesu, kuti moyonso wa Yesu uoneke m'thupi lathu lakufa.
12. Cotero imfa icita mwa ife, koma moyo mwa inu.
13. Koma pokhala nao mzimu womwewo wa cikhulupiriro, monga mwa colembedwaco, ndinakhulupira, cifukwa cace ndinalankhula; ifenso tikhulupira, cifukwa cace tilankhula;
14. podziwa kuti iye amene anaukitsa Ambuye Yesu adzaukitsa ifenso pamodzi ndi Yesu, nadzatiikapo pamodzi ndi inu.