1 Yohane 3:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo yense wakukhala naco ciyembekezo ici pa iye, adziyeretsa yekha, monga Iyeyu ali Woyera.

4. Yense wakucita cimo acitanso kusayeruzika; ndipo cimo ndilo kusayeruzika.

5. Ndipo mudziwa kuti iyeyu anaonekera kudzacotsa macimo; ndipo mwa Iye mulibe cimo.

6. Yense wakukhala mwa iye sacimwa; yense wakucimwa sanamuona iye, ndipo sanamdziwa iye.

7. Tiana, munthu asasokeretse inu; iye wakucita colungama af wolungama, monga Iyeyu ali wolungama:

8. iye wocita cimo ali wocokera mwa mdierekezi, cifukwa mdierekezi amacimwa kuyambira paciyambi. Kukacita ici Mwana wa Mulungu adaonekera, ndiko kuti akaononge nchito za mdierekezi,

1 Yohane 3