11. Pakuti uwu ndi uthenga mudaumva kuyambira paciyambi, kuti tikondane wina ndi mnzace:
12. osati monga Kaini anali wocokera mwa woipayo, namupha mbale wace. Ndipo anamupha iye cifukwa ninji? Popeza nchiro zace zinali zoipa, ndi za mbaie wace zolungama.
13. Musazizwe, abale, Jikadana nanu dziko lapansi.
14. Ife tidziwa kuti tacokera kuturuka muimfa kulowa m'moyo, cifukwa tikondana ndi abale iye amene sakonda akhala muimfa.
15. Yense wakudana ndi mbale wace ali wakupha munthu; ndipo mudziwa kun wakupha munthu ali yense alibe moyo wosatha wakukhala mwa iye.