1 Samueli 3:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo mwanayo Samueli anatumikira Yehova pamaso pa Eli. Ndipo masiku aja mau a Yehova anamveka kamodzi kamodzi; masomphenya sanaoneka-oneka.

2. Ndipo kunali nthawi yomweyo Eli atagona m'malo mwace (maso ace anayamba cizirezire osatha kupenya bwino);

3. ndi nyali ya Mulungu isanazime, Samueli nagona m'Kacisi wa Yehova, m'mene munali likasa la Mulungu.

4. Pamenepo Yehova anaitana Samueli; ndipo iye anayankha kuti, Ndiri pano.

1 Samueli 3