1 Samueli 17:54-57 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

54. Ndipo Davide anatenga mutu wa Mfilistiyo, napita nao ku Yerusalemu; koma zida zace anazisunga m'hema wace.

55. Ndipo pamene Sauli anaona Davide alikuturukira kwa Mfilistiyo, iye anati kwa Abineri, kazembe wa khamu la nkhondo, Abineri, mnyamata uyu ndi mwana wa yani? Nati Abineri, Pali moyo wanu, mfumu, ngati ndidziwa.

56. Ndipo mfumu inati, Ufunsire kuti mnyamatayo ndi mwana wa yani.

57. Ndipo pamene Davide anabwera, atapha Mfilistiyo, Abineri anamtenga, nafika naye pamaso pa Sauli, mutu wa Mfilistiyo uli m'dzanja lace.

1 Samueli 17