1 Samueli 14:23-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Comweco Yehova anapulumutsa Israyeli tsiku lija; ndipo nkhondo inapitirira pa Betaveni.

24. Ndipo Aisrayeli anasauka tsiku lija; pakuti Sauli anawalumbirira, kuti, Atembereredwe iye wakudya kanthu kufikira madzulo, ndikabwezere cilango adani anga. Motero anthu onse anakhala opanda kudya.

25. Ndipo anthu onsewo analowa munkhalango, panali uci pansi.

26. Ndipo pakufika anthuwo m'nkhalangomo, onani, madzi a uci anacuruka; koma panalibe munthu mmodzi anaika dzanja lace pakamwa, pakuti anthuwo anaopa tembererolo.

1 Samueli 14