1 Samueli 10:15-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndipo mbale wa atate wa Sauli anati, Undiuze cimene Samueli analankhula nawe.

16. Ndipo Sauli anati kwa mbale wa atate wace, Anatiuza momveka kuti aburuwo anapezedwa kale. Koma sanamdziwitsa mau aja Samueli ananena zaufumuwo.

17. Ndipo Samueli anaitana anthu onse asonkhane kwa Yehova ku Mizipa;

18. nanena ndi ana a Israyeli, Atero Yehova, Mulungu wa Israyeli kuti, Ine ndinaturutsa Israyeli m'Aigupto, ndipo ndinakupulumutsani m'manja a Aaigupto, ndi m'manja a maufumu onse anakusautsani;

1 Samueli 10