1 Mbiri 9:30-44 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. Ndi ana ena a, ansembe anasanganiza cisanganizo ca zonunkhira,

31. Ndi Matitiya wina wa Alevi, ndiye mwana woyamba wa Salumu Mkora, anaikidwa ayang'anire zokazingidwa m'ziwaya.

32. Ndi ena a abale ao, a ana a Akohati, anayang'anira mkate woonekera, kuukonza masabata onse.

33. Ndipo awa ndi oyimba akuru a nyumba za makolo a Alevi, okhala m'zipinda, omasuka ku nchito zina; pakuti anali nayo nchito yao usana ndi usiku.

34. Awa ndi akuru a nyumba za makolo a Alevi mwa mibadwo yao, ndiwo akuru; anakhala ku Yerusalemu awa.

35. Ndipo m'Gibeoni munakhala atate wa Gibeoni Yeieli, dzina la mkazi wace ndiye Maaka;

36. ndi mwana wace woyamba ndiye Abidoni, opandana naye ndi Zuri, ndi Kisi, ndi Baala, ndi Neri, ndi Nadabu,

37. ndi Gedoro, ndi Ahiya, ndi Zekariya, ndi Mikiloti.

38. Ndi Mikiloti anabala Simeamu. Ndipo iwonso anakhala pamodzi ndi abale ao m'Yerusalemu, pandunji pa abale ao.

39. Ndipo Neri anabala Kisi, ndi Kisi anabala Sauli, ndi Sauli anabala Yonatani, ndi Malikisuwa, ndi Abinadabu, ndi Esbaala.

40. Ndipo mwana wa Yonatani ndiye Meribaala; ndi Meribaala anabala Mika.

41. Ndi ana a Mika: Pitoni, ndi Meleki, ndi Tareya, ndi Ahazi.

42. Ndi Ahazi anabala Yara, ndi Yara anabala Ameleti, ndi Azmaveti, ndi Zimri; ndi Zimri anabala Moza,

43. ndi Moza anabala Bineya, ndi Refaya mwana wace, Eleasa mwana wace; Azeli mwana wace;

44. ndi Azeli anali nao ana asanu ndi mmodzi, maina ao ndi awa; Azrikamu, Bokeru, ndi Ismayeli, ndi Seariya, ndi Obadiya, ndi Hanani; awa ndi ana a Azeli.

1 Mbiri 9