1 Mbiri 9:15-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. ndi Bakabakara, Heresi, ndi Galala, ndi Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zikiri, mwana wa Asafu;

16. ndi Obadiya mwana wa Semaya, mwana wa Galala, mwana wa Yedutuni, ndi Berekiya mwana wa Asa, mwana wa Elikana, wokhala m'midzi ya Anetofati.

17. Ndi odikira pakhomo: Salumu, ndi Akubu, ndi Talimoni, ndi Ahimani ndi abate ao; Salumu ndi mkuru wao,

18. amene adadikira pa cipata ca mfumu kum'mawa mpaka pomwepo, ndiwo odikira pakhomo a tsasa la ana a Levi.

19. Ndipo Salumu mwana wa Kore, mwana wa Ebiasafu; mwana wa Kora, ndi abale ace a nyumba ya atate wace; Akora anayang'anira nchito ya utumiki, osunga zipata za kacisi monga makolo ao; anakhala m'cigono ca Yehova osunga polowera;

20. ndi a Pinehasi mwana wa Eleazara anali mtsogoleri wao kale, ndipo Yehova anali naye.

1 Mbiri 9