5. Ndi abale ao mwa mabanja onse a Isakara, ngwazi zamphamvu, oyesedwa mwa cibadwidwe cao, onsewa ndiwo zikwi zisanu ndi zitatu mphambu zisanu ndi ziwiri.
6. Ana a Benjamini ndiwo Bela, ndi Bekeri, ndi Yedyaeli, atatu.
7. Ndi ana a Bela: Ezboni, ndi Uzi, ndi Uzieli, ndi Yerimoti, ndi hi, asanu; akuru a nyumba za makolo ao, ngwazi zamphamvu, owerengedwa m'mabuku a cibadwidwe zikwi makumi awiri mphambu ziwiri kudza makumi atatu ndi anai.
8. Ndi ana a Bekeri: Zemira, ndi Yoasi, ndi Eliezeri, ndi Eliunai, ndi Omri, ndi Yeremoti, ndi Abiya, ndi Anatoti, ndi Alemeti. Onsewa ndiwo ana a Bekeri.
9. Ndipo anayesedwa mwa cibadwidwe cao, mwa mibadwo yao, akulu a nyumba za makolo ao, ngwazi zamphamvu zikwi makumi awiri mphambu mazana awiri.
10. Ndi mwana wa Yedyaeli: Bilani; ndi ana a Bilani: Yeusi, ndi Benjamini, ndi Ehudi, ndi Kenana, ndi Zetani, ndi Tarasisi, ndi Ahisabara.
11. Onsewa ndiwo ana a Yedyaeli; ndiwo akuru a nyumba za makolo ao, ngwazi zamphamvu zikwi khumi mphambu zisanu ndi ziwiri kudza mazana awiri akuturuka kugulu kunkhondo.
12. Sufimu yemwe ndi Hupimu ana a Iri, ndi Husimu mwana wa Aheri.
13. Ana a Nafuali: Yazieli, ndi Guni, ndi Yezeri, ndi Salumu, ana a Bila.
14. Ana a Manase ndiwo Asrieli amene mkazi wace anambala, Koma mkazi wace wamng'ono Maramu anabala Makiri atate wa Gileadi;
15. ndi Makiri anadzitengera mkazi, mlongo wace wa Hupimu ndi Supimu, dzina lace ndiye Maaka. Ndipo dzina la mwana waciwiri wa Manase ndiye Tselofekadi. Ndi Tselofekadi anali ndi ana akazi.
16. Ndi Maaka mkazi wa Makiri anabala mwana, namucha dzina lace Peresi, ndi dzina la mbale wace ndiye Seresi, ndi ana ace ndiwo Ulamu, ndi Rakemu.
17. Ndi mwana wa Ulamu: Bedani; ndiwo ana a Gileadi mwana wa Makiri mwana wa Manase.
18. Ndi mlongo wace Hamoleketi anabala Isodi, ndi Abiezeri, ndi Mala.
19. Ndi ana a Semida ndiwo Ahiani, ndi Sekemu, ndi Liki, ndi Aniamu.