1 Mbiri 27:2-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Woyang'anira cigawo coyamba ca mwezi, woyamba ndiye Yasobeamu mwana wa Zabidiyeli; m'cigawo mwace munali zikwi makumi awiri mphambu zinai.

3. Ndiye wa ana a Perezi, mkuru wa akazembe onse a khamu mwezi woyamba.

4. Woyang'anira cigawo ca mwezi waciwiri ndiye Dodai M-ahohi ndi cigawo cace; ndi Mikiloti mtsogoleri, ndi m'cigawo cace munali zikwi makumi awiri mphambu zinai.

5. Kazembe wacitatu wa khamu wa mwezi wacitatu ndiye Benaya mwana wa Yehoyada wansembe wamkuru; ndi m'cigawo mwacemunalinso zikwi makumi awiri mphambu zinai.

6. Benaya ameneyo ndiye wamphamvu uja wa makumi atatu aja, woyang'anira makumi atatu aja; woyang'anira cigawo cace ndi Amizabadi mwana wace.

7. Wacinai wa mwezi wacinai ndiye Asebeli mbale wa Yoabu, ndi pambuyo pace Zebadiya mwana wace; ndi m'cigawo mwace munali zikwi makumi awiri mphambu zinai.

8. Kazembe wacisanu wa mwezi wacisanu ndiye Samuti M-izra; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

9. Wacisanu ndi cimodzi wa mwezi wacisanu ndi cimodzi ndiye Ira mwana wa Ikesi Mtekoi; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

1 Mbiri 27