9. Myimbireni, myimbireni zomlemekeza;Fotokozerani zodabwiza zace zonse.
10. Mudzitamandire ndi dzina lace lopatulika;Mitima yao ya iwo ofuna Yehova ikondwere.
11. Funsirani kwa Yehova ndi mphamvu yace;Funani nkhope yace nthawi zonse.
12. Kumbukilani zodabwiza zace adazicita,Zizindikilo zace, ndi maweruzo a pakamwa pace;
13. Inu mbeu ya Israyeli mtumiki wace,Inu ana a Yakobo, osankhika ace.