1 Mbiri 16:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Myimbireni, myimbireni zomlemekeza;Fotokozerani zodabwiza zace zonse.

10. Mudzitamandire ndi dzina lace lopatulika;Mitima yao ya iwo ofuna Yehova ikondwere.

11. Funsirani kwa Yehova ndi mphamvu yace;Funani nkhope yace nthawi zonse.

12. Kumbukilani zodabwiza zace adazicita,Zizindikilo zace, ndi maweruzo a pakamwa pace;

13. Inu mbeu ya Israyeli mtumiki wace,Inu ana a Yakobo, osankhika ace.

1 Mbiri 16