1 Mbiri 16:7-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Tsiku limenelo tsono Davide anayamba kuwapatsa nyimbo ya kuyamika nayo Yehova; ocita ndiwo Asafu ndi abale ace.

8. Yamikani Yehova, itanani dzina lace;Bukitsani mwa mitundu ya anthu zocita iye.

9. Myimbireni, myimbireni zomlemekeza;Fotokozerani zodabwiza zace zonse.

10. Mudzitamandire ndi dzina lace lopatulika;Mitima yao ya iwo ofuna Yehova ikondwere.

11. Funsirani kwa Yehova ndi mphamvu yace;Funani nkhope yace nthawi zonse.

12. Kumbukilani zodabwiza zace adazicita,Zizindikilo zace, ndi maweruzo a pakamwa pace;

13. Inu mbeu ya Israyeli mtumiki wace,Inu ana a Yakobo, osankhika ace.

14. Iye ndiye Yehova Mulungu wathu;Maweruzo ace akhala pa dziko lonse lapansi,

15. Kumbukilani cipangano cace kosatha,Mauwo anawalamulira mibadwo zikwi;

16. Cipanganoco anapangana ndi Abrahamu,Ndi lumbiro lace ndi Isake;

1 Mbiri 16