1 Mbiri 16:6-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. ndi Benaya ndi Yahazieli ansembe ndi malipenga kosalekeza, ku likasa la cipangano la Mulungu.

7. Tsiku limenelo tsono Davide anayamba kuwapatsa nyimbo ya kuyamika nayo Yehova; ocita ndiwo Asafu ndi abale ace.

8. Yamikani Yehova, itanani dzina lace;Bukitsani mwa mitundu ya anthu zocita iye.

9. Myimbireni, myimbireni zomlemekeza;Fotokozerani zodabwiza zace zonse.

10. Mudzitamandire ndi dzina lace lopatulika;Mitima yao ya iwo ofuna Yehova ikondwere.

11. Funsirani kwa Yehova ndi mphamvu yace;Funani nkhope yace nthawi zonse.

12. Kumbukilani zodabwiza zace adazicita,Zizindikilo zace, ndi maweruzo a pakamwa pace;

13. Inu mbeu ya Israyeli mtumiki wace,Inu ana a Yakobo, osankhika ace.

14. Iye ndiye Yehova Mulungu wathu;Maweruzo ace akhala pa dziko lonse lapansi,

15. Kumbukilani cipangano cace kosatha,Mauwo anawalamulira mibadwo zikwi;

16. Cipanganoco anapangana ndi Abrahamu,Ndi lumbiro lace ndi Isake;

17. Ndipo anacitsimikizirakwa Yakobo cikhale malemba,Cikhale cipangano cosatha kwa Israyeli;

18. Ndi kunena kuti, Ndidzakupatsa iwe dziko la Kanani,Gawo la colandira cako;

19. Pokhala inu anthu owerengeka,Inde anthu pang'ono, ndi alendo m'mwemo;

20. Nayendayenda kucokera mtundu wina kufikira mtundu wina,Kucokera ufumu wina kufikira anthu ena.

21. Sanalola munthu awasautse;Ndipo anadzudzula mafumu cifukwa ca iwowa;

22. Ndi kuti, Musamakhudza odzozedwa anga,Musamacitira coipa aneneri anga,

1 Mbiri 16