6. ndi Benaya ndi Yahazieli ansembe ndi malipenga kosalekeza, ku likasa la cipangano la Mulungu.
7. Tsiku limenelo tsono Davide anayamba kuwapatsa nyimbo ya kuyamika nayo Yehova; ocita ndiwo Asafu ndi abale ace.
8. Yamikani Yehova, itanani dzina lace;Bukitsani mwa mitundu ya anthu zocita iye.
9. Myimbireni, myimbireni zomlemekeza;Fotokozerani zodabwiza zace zonse.
10. Mudzitamandire ndi dzina lace lopatulika;Mitima yao ya iwo ofuna Yehova ikondwere.
11. Funsirani kwa Yehova ndi mphamvu yace;Funani nkhope yace nthawi zonse.
12. Kumbukilani zodabwiza zace adazicita,Zizindikilo zace, ndi maweruzo a pakamwa pace;
13. Inu mbeu ya Israyeli mtumiki wace,Inu ana a Yakobo, osankhika ace.
14. Iye ndiye Yehova Mulungu wathu;Maweruzo ace akhala pa dziko lonse lapansi,
15. Kumbukilani cipangano cace kosatha,Mauwo anawalamulira mibadwo zikwi;
16. Cipanganoco anapangana ndi Abrahamu,Ndi lumbiro lace ndi Isake;
17. Ndipo anacitsimikizirakwa Yakobo cikhale malemba,Cikhale cipangano cosatha kwa Israyeli;
18. Ndi kunena kuti, Ndidzakupatsa iwe dziko la Kanani,Gawo la colandira cako;
19. Pokhala inu anthu owerengeka,Inde anthu pang'ono, ndi alendo m'mwemo;
20. Nayendayenda kucokera mtundu wina kufikira mtundu wina,Kucokera ufumu wina kufikira anthu ena.
21. Sanalola munthu awasautse;Ndipo anadzudzula mafumu cifukwa ca iwowa;
22. Ndi kuti, Musamakhudza odzozedwa anga,Musamacitira coipa aneneri anga,