39. ndi Zadoki wansembe, ndi abale ace ansembe, ku kacisi wa Yehova, pa msanje unali ku Gibeoni;
40. kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa guwa la nsembe zopsereza, kosalekeza, m'mawa ndi madzulo, monga mwa zonse zilembedwa m'cilamulo ca Yehova adacilamulira Israyeli;
41. ndi pamodzi nao Hemani, ndi Yedutuni, ndi osankhika otsalawo, ochulidwa maina, kuyamika Yehova; pakuti cifundo cace ncosatha;
42. ndi pamodzi nao Hemani, ndi Yedutuni, ndi malipenga ndi nsanje za iwo akumveketsadi, ndi zoyimbira nyimbo za Mulungu; ndi ana a Yedutuni anakhala kucipata.
43. Ndipo anacoka anthu onse, yense ku nyumba yace, nabwera Davide kudalitsa nyumba yace.