22. Ndi kuti, Musamakhudza odzozedwa anga,Musamacitira coipa aneneri anga,
23. Myimbireni Yehova, inu dziko lonse lapansi,Lalikirani cipulumutso cace tsiku ndi tsiku,
24. Fotokozerani ulemerero wace mwa amitundu,Zodabwiza zace mwa mitundu yonse ya anthu.
25. Pakuti Yehova ali wamkuru, nayenera kulemekezedwa kwakukulu;Ayenera amuope koposa milungu yonse.