1 Mbiri 16:18-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndi kunena kuti, Ndidzakupatsa iwe dziko la Kanani,Gawo la colandira cako;

19. Pokhala inu anthu owerengeka,Inde anthu pang'ono, ndi alendo m'mwemo;

20. Nayendayenda kucokera mtundu wina kufikira mtundu wina,Kucokera ufumu wina kufikira anthu ena.

21. Sanalola munthu awasautse;Ndipo anadzudzula mafumu cifukwa ca iwowa;

22. Ndi kuti, Musamakhudza odzozedwa anga,Musamacitira coipa aneneri anga,

23. Myimbireni Yehova, inu dziko lonse lapansi,Lalikirani cipulumutso cace tsiku ndi tsiku,

24. Fotokozerani ulemerero wace mwa amitundu,Zodabwiza zace mwa mitundu yonse ya anthu.

25. Pakuti Yehova ali wamkuru, nayenera kulemekezedwa kwakukulu;Ayenera amuope koposa milungu yonse.

26. Pakuti milungu ya mitundu ya anthu ndiyo mafano;Koma Yehova analenga zakumwamba.

1 Mbiri 16