1 Mbiri 16:16-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Cipanganoco anapangana ndi Abrahamu,Ndi lumbiro lace ndi Isake;

17. Ndipo anacitsimikizirakwa Yakobo cikhale malemba,Cikhale cipangano cosatha kwa Israyeli;

18. Ndi kunena kuti, Ndidzakupatsa iwe dziko la Kanani,Gawo la colandira cako;

19. Pokhala inu anthu owerengeka,Inde anthu pang'ono, ndi alendo m'mwemo;

20. Nayendayenda kucokera mtundu wina kufikira mtundu wina,Kucokera ufumu wina kufikira anthu ena.

21. Sanalola munthu awasautse;Ndipo anadzudzula mafumu cifukwa ca iwowa;

22. Ndi kuti, Musamakhudza odzozedwa anga,Musamacitira coipa aneneri anga,

23. Myimbireni Yehova, inu dziko lonse lapansi,Lalikirani cipulumutso cace tsiku ndi tsiku,

1 Mbiri 16