55. Naimirira, nadalitsa msonkhano wonse wa Israyeli ndi mau okweza, nati,
56. Wolemekezeka ndi Yehova amene anapumulitsa anthu ace Aisrayeli, monga mwa zonse analonjezazo; sanatayika mau amodzi a mau ace onse abwino, amene analankhula ndi dzanja la Mose mtumiki wace.
57. Yehova Mulungu wathu akhale nafe monga umo anakhalira nao makolo athu, asatisiye kapena kutitaya;
58. kuti atitembenuzire kwa iye yekha mitima yathu iyende m'njira zace zonse, ndi kusunga malamulo ace onse ndi malemba ace ndi maweruzo ace, amene anawalamulira makolo athu.