Zekariya 8:21-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. ndi okhala m'mudzi umodzi adzamuka ku mudzi wina, ndi kuti, Tiyeni msanga kukapepeza Yehova, ndi kufunafuna Yehova wa makamu; ndimuka inenso.

22. Inde, mitundu yambiri ya anthu, ndi amitundu amphamvu adzadza kufunafuna Yehova wa makamu m'Yerusalemu, ndi kupepeza Yehova.

23. Atero Yehova wa makamu: Kudzacitika masiku awo amuna khumi adzagwira, ndiwo a manenedwe onse a amitundu, inde adzagwira mkawo wa munthu ali Myuda, ndi kuti, Tidzamuka nanu, pakuti tamva kuti Mulungu ali ndi inu.

Zekariya 8