Zefaniya 3:12-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Koma ndidzasiya pakati pako anthu ozunzika ndi osauka, ndipo iwo adzakhulupirira dzina la Yehova.

13. Otsala a Israyeli sadzacita cosalungama, kapena kunena mabodza; ndi m'kamwa mwao simudzapezeka lilime lonyenga; pakuti adzadya nadzagona pansi, ndi palibe wakuwaopsa.

14. Yimba, mwana wamkazi wa Ziyoni; pfuula, Israyeli; kondwera nusekerere ndi mtima wonse, mwana wamkazi wa Yerusalemu.

15. Yehova wacotsa maweruzo ako, anataya kunja mdani wako; mfumu ya Israyeli, Yehova, ali pakati pako, sudzaopanso coipa.

Zefaniya 3