6. Ndipo Yoswa anati kwa ansembe, Senzani likasa la cipangano, nimuoloke pamaso pa anthu. Nasenza iwo likasa la cipangano, natsogolera anthu.
7. Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, Lero lino ndidzayamba kukukuza pamaso pa Aisrayeli onse, kuti adziwe, kuti monga momwe ndinakhalira ndi Mose, momwemo ndidzakhala ndi iwe.
8. Ndipo uzilamulira ansembe akunyamula likasa la cipangano, ndi kuti, Pamene mufika kumphepete kwa madzi a Yordano muziima m'Yordano.