28. Pamenepo Yoswa anauza anthu amuke, yense ku colowa cace.
29. Ndipo kunali, zitatha izi, Yoswa mwana wa Nuni mtumiki wa Yehova, adafa, wa zaka zana ndi khumi.
30. Ndipo anamuika m'malire a colowa cace m'Timinati-sera, ndiwo ku mapiri a Efraimu kumpoto kwa phiri la Gaasi.
31. Ndipo Israyeli anatumikira Yehova masiku onse a Yoswa, ndi masiku onse a akulu akulu otsala atafa Yoswa, amene anadziwa nchito yonse ya Yehova anaicitira Israyeli.