Yoswa 24:24-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Ndipo anthu anati kwa Yoswa, Tidzamtumikira Yehova Mulungu wathu ndi kumvera mau ace.

25. Motero Yoswa anacita pangano ndi anthu tsiku lija, nawaikira lemba ndi ciweruzo m'Sekemu.

26. Ndipo Yoswa analembera mau awa m'buku la cilamulo ca Mulungu; natenga mwala waukuru, nauimitsa apo patsinde pa thundu wokhala pa malo opatulika a Yehova.

27. Ndipo Yoswa anati kwa anthu onse, Taonani, mwala uwu udzakhala mboni yotitsutsa; pakuti udamva mau onse a Yehova amene ananena kwa ife; ndipo udzakhala mboni yotsutsa inu, mungakanize Mulungu wanu.

28. Pamenepo Yoswa anauza anthu amuke, yense ku colowa cace.

29. Ndipo kunali, zitatha izi, Yoswa mwana wa Nuni mtumiki wa Yehova, adafa, wa zaka zana ndi khumi.

Yoswa 24