Yohane 6:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. N ati Yesu, Akhalitseni anthu pansi, Ndipo panali udzu wambiri pamalopo, Pamenepo amunawo anakhala pansi, kuwerenga kwao monga zikwi zisanu.

11. Pomwepo Yesu anatenga mikateyo; ndipo pamene adayamika, anagawira iwo akukhala pansi; momwemonso ndi tinsomba, monga momwe iwo anafuna.

12. Ndipo pamene adakhuta, Iyeananena kwa akuphunzira ace, Sonkhanitsani makombo kuti kasatayike kanthu.

13. Pomwepo anasonkhanitsa, nadzaza mitanga khumi ndi iwiri ndi makombo a mikate isanuyo yabarele, amene anatsalira anadyawo.

14. Cifukwa cace, anthu, poona cizindikilo cimene anacita, ananena, kuti, Ameneyo ndiye mneneri ndithu wakudzayom'dziko lapansi.

Yohane 6