4. Koma pakuyamba kuca, Yesu anaimirira pam bali pa nyanja, komatu akuphunzirawo sanadziwa kuti ndiye Yesu.
5. Yesu ananena nao, Ananu, muli nako kanthu kakudya kodi? Anamyankha iye, lai.
6. Koma anati kwa iwo, Ponyani khoka ku mbali ya dzanja lamanja ya ngalawa, ndipo mudzapeza, Pamenepo anaponya, ndipo analibenso mphamvu yakulikoka cifukwa ca kucuruka nsomba.