18. Cifukwa ca icinso khamulo linadza kudzakomana ndi iye, cifukwa anamva kuti iye adacita cizindikilo ici.
19. Cifukwa cace Afarisi ananena wina ndi mnzace, Muona kuti simupindula kanthu konse; onani dziko litsata pambuyo pace pa iye.
20. Koma panali Ahelene ena mwa iwo akukwera kunka kukalambira paphwando,
21. Ndipo iwo anadza kwa Filipo wa ku Betsaida wa m'Galileya, namfunsa iye, ndi kuti, Mbuye, tifuna kuona Yesu.