Yohane 10:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Iye wosalowa m'khola la nkhosa pakhomo, koma akwerera kwina, iyeyu ndiye wakuba ndi wolanda.

2. Koma iye wakulowera pakhomo, ndiye mbusa wa nkhosa.

3. Iyeyu, wapakhomo amtsegulira ndi nkhosa zimva mau ace; ndipo aitana nkhosa za iye yekha maina ao, nazitsogolera kunja.

4. Pamene adaturutsa zonse za iye yekha, azitsogolera; ndi nkhosa zimtsata iye; cifukwa zidziwa mau ace.

5. Koma mlendo sizidzamtsata, koma zidzamthawa; cifukwasizidziwa mau a alendo.

Yohane 10