Yohane 1:36-40 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

36. ndipo poyang'ana Yesu alikuyenda, anati, 10 Onani Mwanawankhosa wa Mulungu!

37. Ndipo akuphunzira awiriwo anamva iye alinkulankhula, natsata Yesu.

38. Koma Yesu anaceuka, napenya iwo alikumtsata, nanena nao, Mufuna ciani? Ndipo anati kwa iye, Rabi (ndiko kunena posandulika, Mphunzitsi), mukhala kuti?

39. Nanena nao, Tiyeni, mukaone, Pamenepo anadza naona kumene anakhala; nakhala ndi iye tsiku lomwelo; panali monga ora lakhumi.

40. Andreya mbale wace wa Simoni Petro anali mmodzi wa awiriwo, anamva Yohane, namtsata iye.

Yohane 1