Yobu 9:29-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Mlandu udzanditsutsa;Potero ndigwire nchito cabe cifukwa ninji?

30. Ndikasamba madzi a cipale cofewaNdi kuyeretsa manja anga ndi sopo;

31. Mudzandibviikanso muli zoola,Ndi zobvala zanga zidzanyansidwa nane.

32. Pakuti sindiye munthu, monga ine, kuti ndimyankhe,Kuti tikomane mlandu.

33. Palibe wakutiweruza,Wakutisanjika ife tonse awiri manja ace.

Yobu 9