Yesaya 5:1-2 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndiyimbire wokondedwa wanga nyimbo ya wokondedwa wanga ya munda wace wamphesa, Wokondedwa wanga anali ndi munda wamphesa m'citunda ca zipatso zambiri;

2. ndipo iye anakumba mcerenje kuzungulira kwete, natolatola miyala pamenepo naokapo mpesa wosankhika, namangapo pakati pace nsanja, nasema mopondera mphesa, nayembekeza kuti udzabala mphesa, koma unangobala mphesa zosadya.

Yesaya 5